2 Mafumu 21:20-26 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Nacita iye coipa pamaso pa Yehova, monga umo amacitira Manase atate wace.

21. Nayenda iye m'njira monse anayendamo atate wace, natumikira mafano anawatumikira atate wace, nawagwadira;

22. nasiya Yehova Mulungu wa makolo ace, sanayenda m'njira ya Yehova.

23. Ndipo anyamata ace a Amoni anamcitira ciwembu, napha mfumuyo m'nyumba yace yace.

24. Koma anthu a m'dzikomo anapha onse akumcitira ciwembu mfumu Amoni; ndipo anthu a m'dzikomo anamlonga ufumu Yosiya mwana wace m'malo mwace.

25. Macitidwe ena tsono a Amoni adawacita, salembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Yuda?

26. Naikidwa iye m'manda mwace m'munda wa Uza; nakhalamfumum'malo mwace Yosiya mwana wace.

2 Mafumu 21