10. Nadziimikira zoimiritsa ndi zifanizo pa citunda ciri conse cacitali, ndi patsinde pa mtengo uli wonse wogudira;
11. nafukizapo zonunkhira pa misanje youse, monga umo amacitira amitundu amene Yehova adawacotsa pamaso pao, nacita zoipa kuutsa mkwiyo wa Yehova;
12. natumikira mafano amene Yehova anawanena nao, Musacita ici.