18. Nacita coipa pamaso pa Yehova masiku ace onse, osaleka zolakwa za Yerobiamu mwana wa Nebati, zimene analakwitsa nazo Israyeli.
19. Pamenepo Puli mfumu ya Asuri anadza kudzamenyana ndi dziko, koma Menahemu anampatsa Puli matalente a siliva cikwi cimodzi; kuti dzanja lace likhale naye kukhazikitsa ufumu m'dzanja lace.
20. Ndipo Menahemu anasonkhetsa Israyeli ndaramazi, nasonkhetsa acuma, yense masekeli makumi asanu a siliva: kuti azipereke kwa mfumu ya Asuri. Nabwerera mfumu ya Asuri osakhala m'dzikomo.