2 Mafumu 13:8-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Macitidwe ena tsono a Yoahazi, ndi zonse anazicita, ndi mphamvu yace, sizilembedwa kodi m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

9. Ndipo Yoahazi anagona ndi makolo ace, namuika m'Samariya; nakhala mfumu m'malo mwace Yoasi mwana wace.

10. Caka ca makumi atatu ndi zisanu ndi ziwiri ca Yoasi mfumu ya Yuda, Yoasi mwana wa Yoahazi analowa ufumu wace wa Israyeli m'Samariya, nakhala mfumu zaka khumi ndi zisanu ndi cimodzi.

11. Nacita coipa pamaso pa Yehova, osazileka zolakwa zonse za Yerobiamu mwana wa Nebati, zimene analakwitsa nazo Israyeli, koma anayendamo.

2 Mafumu 13