2 Akorinto 11:29-33 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

29. 3 Afoka ndani wosafoka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

30. Ngati ndiyenerakudzitamandira, 4 ndidzadzitamandira ndi za kufoka kwanga.

31. Mulungu Atate wa Ambuye Yesu, iye amene alemekezeka ku nthawi yonse, adziwa kuti sindinama.

32. M'Damasiko kazembe wa mfumu Areta analindizitsa mudzi wa Adamasiko kuti andigwire ine;

33. ndipo mwa zenera, mumtanga, ananditsitsa pakhoma, ndipo ndinapulumuka m'manja mwace.

2 Akorinto 11