2 Akorinto 11:24-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Kwa Ayuda ndinalandirakasanu mikwingwirima makumi anai kuperewera umodzi.

25. Katatu ndinamenyedwa ndi ndodo, kamodzi ndinaponyedwa miyala, katatu ndinatayika posweka combo, ndinakhala m'kuya tsiku limodzi usana ndi usiku;

26. paulendo kawiri kawiri, moopsya mwace mwa mitsinje, moopsya mwace mwa olanda, 1 moopsya modzera kwa mtundu wanga, moopsya modzera kwa amitundu, moopsya m'mudzi, moopsya m'cipululu, moopsya m'nyanja, moopsya mwaabale onyenga;

27. m'cibvutitso ndi m'colemetsa, m'madikiro kawiri kawiri, 2 m'njala ndi ludzu, m'masalo a cakudyakawiri kawiri, m'cisanu ndi umarisece.

28. Popanda zakunjazo pali condisindikiza tsiku ndi tsiku, calabadiro ca Mipingo yonse.

29. 3 Afoka ndani wosafoka inenso? Akhumudwitsidwa ndani, wosatenthanso ine?

2 Akorinto 11