1 Samueli 8:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pamene Samueli anakalamba, anaika ana ace amuna akhale oweruza a Israyeli.

2. Dzina la mwana wace woyamba ndiye Yoeli, ndi dzina la waciwiri ndiye Abiya; ndiwo oweruza a ku Beereseba.

3. Ndipo ana ace sanatsanza makhalidwe ace, koma anapambukira ku cisiriro, nalandira cokometsera mlandu, naipitsa kuweruza.

4. Pamenepo akuru onse a Israyeli anasonkhana, nadza kwa Samueli ku Rama;

5. nanena naye, Taonani, mwakalamba, ndipo ana anu satsanza makhalidwe anu; tsono, mutilongere mfumu kuti ikatiweruze, monga umo mucitidwa m'mitundu yonse ya anthu.

1 Samueli 8