1 Samueli 31:10-13 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo anaika zida zace m'nyumba ya Asitarote; napacika mtembo wace ku linga la ku Betisani.

11. Koma pamene a ku Jabezi Gileadi anamva zimene Afilisti anamcitira Sauli,

12. ngwazi zonse zinanyamuka ndi kucezera usiku kuyenda, natenga mtembo wa Sauli, ndi mitembo ya ana ace, pa linga la Betisani; nafika ku Jabezi Gileadi naitentha kumeneko.

13. Natenga mafupa ao nawaika patsinde pa mtengo uli m'Jabezi, nasala kudya masiku asanu ndi awiri.

1 Samueli 31