1 Samueli 25:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Tsono dzina la munthuyo ndiye Nabala, ndi dzina la mkazi wace ndiye Abigayeli; ndiye mkazi wa nzeru yabwino, ndi wa nkhope yokongola; koma mwamunayo anali waphunzo ndi woipa macitidwe ace; ndipo iye anali wa banja la Kalebi.

4. Ndipo Davide anamva kucipululu kuti Nabala alinkusenga nkhosa zace.

5. Davide natuma anyamata khumi, nanena kwa anyamatawo, Mukwere ku Karimeli, mumuke kwa Nabala ndi kundilankhulira iye;

6. ndipo muzitero kwa wodalayo, Mtendere ukhale pa inu, mtendere ukhalenso pa nyumba yanu, ndi mtendere ukhale pa zonse muli nazo.

1 Samueli 25