1 Samueli 23:7-10 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo anthu anauza Sauli kuti Davide wafika ku Keila. Ndipo Sauli anati, Mulungu wampereka m'dzanja langa; pakuti atsekerezeka, popeza analowa m'mudzi wa zitseko ndi mipiringidzo.

8. Ndipo Sauli anamemeza anthu onse kunkhondo, kuti atsikire ku Keila, kumangira misasa Davide ndi anthu ace.

9. Ndipo Davide anadziwa kuti Sauli analikulingalira zomcitira zoipa; nati kwa Abyatara wansembe, Bwera kuno ndi efodi.

10. Nati Davide, Yehova, Mulungu wa Israyeli, mnyamata wanu wamva zoona kuti Sauli afuna kudza ku Keila, kuononga mudziwo cifukwa ca ine.

1 Samueli 23