13. Ndipo ana atatu akuru a Jese anatsata Sauli kunkhondoko; ndi maina ao a ana ace atatuwo adapita ku nkhondowo ndiwo Eliabu woyambayo, ndi mnzace womponda pamutu pace Abinadabu, ndi wacitatu Sama.
14. Ndipo Davide anali wotsiriza; ndi akuru atatuwo anamtsata Sauli.
15. Koma Davide akamuka kwa Sauli, nabwerera kudzadyetsa nkhosa za atate wace ku Betelehemu.