1 Samueli 16:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Ndipo Davide anafika kwa Sauli, naima pamaso pace; ndipo iye anamkonda kwambiri, namsandutsa wonyamula zida zace.

22. Ndipo Sauli anatumiza kwa Jese, nati, Ulole kuti Davide aime pamaso panga; pakuti ndamkomera mtima.

23. Ndipo kunali kuti pamene mzimu woipawo wocokera kwa Mulungu unali pa Sauli, Davide anatenga zeze, naliza ndi dzanja lace; comweco Sauli anatsitsimuka, nakhala bwino, ndi mzimu woipa unamcokeraiye.

1 Samueli 16