21. Ndipo Davide anafika kwa Sauli, naima pamaso pace; ndipo iye anamkonda kwambiri, namsandutsa wonyamula zida zace.
22. Ndipo Sauli anatumiza kwa Jese, nati, Ulole kuti Davide aime pamaso panga; pakuti ndamkomera mtima.
23. Ndipo kunali kuti pamene mzimu woipawo wocokera kwa Mulungu unali pa Sauli, Davide anatenga zeze, naliza ndi dzanja lace; comweco Sauli anatsitsimuka, nakhala bwino, ndi mzimu woipa unamcokeraiye.