1 Samueli 14:44-47 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

44. Pamenepo Sauli anati, Mulungu andilange, naoniezereko, pakuti udzafa ndithu, Jonatani.

45. Ndipo anthuwo ananena ndi Sauli, Kodi Jonatani adzafa, amene anacititsa cipulumutso cacikuru ici m'Israyeli? Musatero. Pali Yehova, palibe tsitsi limodzi la pa mutu wace lidzagwa pansi, pakuti iye anagwirizana ndi Mulungu lero. Comweco anthuwo anapulumutsa Jonatani kuti angafe. Ndipo Sauli analeka kuwapitikitsa Afilistiwo;

46. ndi Afilistiwo anamuka ku malo a iwo okha.

47. Ndipo pamene Sauli atakhazikitsa ufumu wa pa Israyeli, iye anaponyana ndi adani ace onse pozungulira ponse, ndi Moabu, ndi ana a Amoni, ndi Edomu ndi mafumu a Zoba, ndi Afilisti; ndipo pali ponse anapotolokerapo, anawalanga.

1 Samueli 14