1 Samueli 12:20-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo Samueli ananena kwa anthuwo, Musaope; munacitadi coipa ici conse, koma musaleka kutsata Yehova, koma mutumikire Yehova ndi mtima wanu wonse;

21. musapambukire inu kutsata zinthu zacabe, zosapindulitsa, zosapulumutsa, popeza ziri zopanda pace.

22. Pakuti Yehova sadzasiya anthu ace cifukwa ca dzina lace lalikuru; pakuti kudamkomera Yehova kukuyesani inu anthu a iye yekha.

23. Ndipo inenso, kukhale kutali ndi ine, kucimwira Yehova ndi kuleka kukupemphererani; koma ndidzakulangizani njira yabwino ndi yolungama.

1 Samueli 12