33. Ndipo awa ndi oyimba akuru a nyumba za makolo a Alevi, okhala m'zipinda, omasuka ku nchito zina; pakuti anali nayo nchito yao usana ndi usiku.
34. Awa ndi akuru a nyumba za makolo a Alevi mwa mibadwo yao, ndiwo akuru; anakhala ku Yerusalemu awa.
35. Ndipo m'Gibeoni munakhala atate wa Gibeoni Yeieli, dzina la mkazi wace ndiye Maaka;