5. Mika mwana wace, Reaya mwana wace, Baala mwana wace,
6. Beera mwana wace, amene Tigilati Pilesere wa ku Asuri anamtenga ndende; ndiye kalonga wa Arubeni.
7. Ndi abale ace monga mwa mabanja ao, powerenga cibadwidwe ca mibadwo yao: akuru ndiwo Yeyeli, ndi Zekariya,
8. ndi Bela mwana wa Azazi, mwana wa Sema, mwana wa Yoeli, wokhala ku Aroeri, ndi kufikira ku Nebo ndi Baala-meoni;
9. ndi kum'mawa anakhala mpaka polowera kucipululu kuyambira mtsinje wa Firate; pakuti zoweta zao zinacuruka m'dziko la Gileadi.
10. Ndipo masiku a Sauli anagwirana nkhondo ndi Ahagiri, amene adagwa ndi dzanja lao; ndipo anakhala m'mahema mwao kum'mawa konse kwa Gileadi.
11. Ndi ana a Gadi anakhala pandunji pao m'dziko la Basana mpaka Saleka: