1 Mbiri 29:26-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. Momwemo Davide mwana wa Jese adakhala mfumu ya Aisrayeli onse.

27. Ndipo nthawi yoti anakhala mfumu ya Israyeli ndiyo zaka makumi anai; zaka zisanu ndi ziwiri anakhala mfumu m'Hebroni, ndi zaka makumi atatu anakhala mfumu m'Yerusalemu.

28. Nafa atakalamba bwino, wocuruka masiku, zolemera, ndi ulemerero; ndi Solomo mwana wace anakhala mfumu m'malo mwaceo

29. Zocita mfumu Davide tsono, zoyamba ndi zotsiriza, taonani, zalembedwa m'buku la mau a Samueli mlauli, ndi m'buku la mau a Natani mneneri, ndi m'buku la mau a Gadi mlauli;

30. pamodzi ndi za ufumu wace wonse, ndi mphamvu yace, ndi za nthawizo zidampitira iye, ndi Israyeli, ndimaufumu onse a maiko.

1 Mbiri 29