1 Mbiri 26:15-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Obedi Edomu kumwela, ndi ana ace nyumba ya akatundu.

16. Supimu ndi Hosa kumadzulo, ku cipata ca Saleketi, ku mseu wokwerapo, udikiro pandunji pa udikiro.

17. Kum'mawa kunali Alevi asanu ndi mmodzi, kumpoto anai tsiku ndi tsiku, kumwela anai tsiku ndi tsiku, ndi a nyumba ya akatundu awiri ndi awiri.

18. Ku Parabara kumadzulo anai kumseu, ndi awiri ku Parabara.

19. Awa ndi magawidwe a odikira; a ana a Akora, ndi a ana a Merari.

20. Ndipo wa Alevi, Ahiya anayang'anira cuma ca nyumba ya Mulungu, ndi cuma ca zopatulika.

21. Ana a Ladani: ana a Ladani a Agerisoni, akuru a nyumba za makolo a Ladani Mgerisoni, Yehieli.

22. Ana a Yehieli: Zetamu ndi Yoeli mbale wace, oyang'anira cuma ca nyumba ya Yehova.

23. A Amirami, a Aizari, a Ahebroni, a Auziyeli;

24. ndi Sebueli mwana wa Gerisomu, mwana wa Mose, ndiye mkuru woyang'anira zuma.

1 Mbiri 26