1 Mbiri 18:1-3 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo zitatha izi, Davide anakantha Afilisti, nawagonjetsa, nalanda Gati ndi midzi yace m'manja a Afilisti.

2. Anakanthanso Moabu; ndi Amoabu anakhala anthu a Davide, nabwera nazo mphatso,

3. Ndipo Davide anakantha Hadarezeri mfumu ya Zoba ku Hamati, pomuka iye kukhazikitsa ulamuliro wace ku mtsinje wa Firate.

1 Mbiri 18