1 Mbiri 16:24-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

24. Fotokozerani ulemerero wace mwa amitundu,Zodabwiza zace mwa mitundu yonse ya anthu.

25. Pakuti Yehova ali wamkuru, nayenera kulemekezedwa kwakukulu;Ayenera amuope koposa milungu yonse.

26. Pakuti milungu ya mitundu ya anthu ndiyo mafano;Koma Yehova analenga zakumwamba.

27. Pamaso pace pali ulemu ndi ukulu,M'malo mwace muli mphamvu ndi cimwemwe.

28. Mcitireni Yehova, inu mafuko a mitundu ya anthu,Mcitireni Yehova ulemerero ndi mphamvu.

29. Mcitireni Yehova ulemerero wa dzina lace;Bwerani naco copereka, ndipo fikani pamaso pace;Lambirani Yehova m'ciyero cokometsetsa,

30. Njenjemerani pamaso pace, inu dziko lonse lapansi,Dziko lokhalamo anthu lomwe lakhazikika, kuti silingagwedezeke.

31. Kukondwerere kumwamba, ndi dziko lapansi lisekerere;Anene mwa amitundu, Yehova acita ufumu.

32. Nyanja ikukume m'kudzala kwace,Munda ukondwerere, ndi zonse ziri m'mwemo;

33. Pamenepo mitengo yonse ya kunkhalango idzapfuula mokondwera pamaso pa Yehova;Pakuti akudza kudzaweruza dziko lapansi,

34. Yamikani Yehova; pakuti iye ndiye wabwino;Pakuti cifundo cace ncosatha.

1 Mbiri 16