13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.
14. Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,
15. Kumbukilani cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;
16. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;
17. Ndipo anacitsimikizirakwa Yakobo cikhale malemba,Cikhale cipangano cosatha kwa Israyeli;
18. Ndi kunena kuti, Ndidzakupatsa iwe dziko la Kanani,Gawo la colandira cako;
19. Pokhala inu anthu owerengeka,Inde anthu pang'ono, ndi alendo m'mwemo;
20. Nayendayenda kucokera mtundu wina kufikira mtundu wina,Kucokera ufumu wina kufikira anthu ena.
21. Sanalola munthu awasautse;Ndipo anadzudzula mafumu cifukwa ca iwowa;
22. Ndi kuti, Musamakhudza odzozedwa anga,Musamacitira coipa aneneri anga,