1 Mbiri 16:13-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

13. Inu mbeu ya Israyeli mtumiki wace,Inu ana a Yakobo, osankhika ace.

14. Iye ndiye Yehova Mulungu wathu;Maweruzo ace akhala pa dziko lonse lapansi,

15. Kumbukilani cipangano cace kosatha,Mauwo anawalamulira mibadwo zikwi;

16. Cipanganoco anapangana ndi Abrahamu,Ndi lumbiro lace ndi Isake;

1 Mbiri 16