1 Mbiri 12:26-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

26. A ana a Levi zikwi zinai mphambu mazana asanu ndi limodzi.

27. Ndipo Yehoyada, ndiye mtsogoleri wa Aaroni, ndi pamodzi nave zikwi zitatu mphambu mazana asanu ndi awiri;

28. ndi Zadoki, ndiye mnyamata, ngwazi yamphamvu, ndi a nyumba ya kholo lace, akuru makumi awiri mphambu awfri.

29. Ndi a ana a Benjamini, abale a Sauli, zikwi zitatu; pakuti mpaka pomwepo ocuruka a iwowa anaumirira nyumba ya Sauli.

30. Ndi a ana a Efraimu zikwi makumi awiri mphambu mazana asanu ndi atatu, ngwazi zamphamvu, anthu omveka m'nyumba za makolo ao.

31. Ndipo a pfuko la Manase logawika pakati zikwi khumi mphambu zisanu ndi zitatu, ochulidwa maina ao kuti adzalonge Davide mfumu.

32. Ndi a ana a Isakara, anthu akuzindikira nyengo, akudziwa zoyenera Israyeli kuzicita, akuru ao ndiwo mazana awiri; ndi abale ao onse anapenyerera pakamwa pao.

33. A Zebuloni akuturuka kukhamu, opangira nkhondo, monga mwa zida ziri zonse za nkhondo, zikwi makumi asanu, akusunga malongosoledwe a nkhondo ndi mtima wosatekeseka.

34. Ndi a Nafitali atsogoleri cikwi cimodzi, ndi pamodzi nao ogwira zikopa ndi mikondo zikwi makumi atatu mphambu zisanu ndi ziwiri.

1 Mbiri 12