1 Mafumu 21:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Koma panalibe wina ngati Ahabu wakudzigulitsa kucita coipa pamaso pa Yehova, amene Yezebeli mkazi wace anamfulumiza.

26. Ndipo anacita moipitsitsa kutsata mafano, monga mwa zonse amazicita Aamori, amene Yehova adawapitikitsa pamaso pa ana a Israyeli.

27. Ndipo kunali, pakumva Ahabu mau amenewa, anang'amba zobvala zace, nabvala ciguduli pathupi pace, nasala kudya, nagona paciguduli, nayenda nyang'anyang'a.

28. Pamenepo mau a Yehova anadza kwa Eliya wa ku Tisibe, nati,

29. Waona umo wadzicepetsera Ahabu pamaso panga? Popeza adzicepetsa pamaso panga, sindidzafikitsa coipa cimeneci akali moyo iye; koma m'masiku a mwana wace ndidzacifikitsa pa nyumba yace.

1 Mafumu 21