14. Pomwepo anatuma mau kwa Yezebeli, nati, Naboti waponyedwa miyala, nafa.
15. Ndipo kunali, atamva Yezebeli kuti anamponya Naboti miyala nafa, Yezebeli anati kwa Ahabu, Taukani, landirani munda wamphesa wa Naboti Myezreeli uja anakana kukugulitsani ndi ndarama, popeza, Naboti sali ndi moyo, koma wafa.
16. Ndipo kunali, atamva Ahabu kuti Naboti wafa, Ahabu anauka kukatsikira ku munda wamphesa wa Naboti, kuulandira.
17. Ndipo mau a Yehova anadza kwa Eliya waku Tisibe, nati,