7. Ndipo Obadiya ali m'njira, taona, Eliya anakomana naye; iye namdziwa, namgwadira, nati, Ndinu kodi mbuye wanga Eliya?
8. Ndipo anamyankha, nati, Ndine amene; kauze mbuye wako kuti Eliya wabwera,
9. Iye nati, Ndacimwanji kuti mupereka kapolo wanu m'dzanja la Ahabu kundipha?
10. Pali Yehova Mulungu wanu, ngati kuli mtundu umodzi wa anthu, kapena ufumu, kumene mbuye wanga sanatumako kukufunani, ndipo pakunena iwo, Palibe iye, analumbiritsa ufumu umene ndi mtundu umene kuti sanakupezani.
11. Ndipo tsopano mukuti, Kauze mbuye wako kuti Eliya wabwera.