1 Mafumu 18:20-25 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pamenepo Ahabu anatumiza mau kwa ana onse a Israyeli, namemeza aneneri onse ku phiri la Karimeli.

21. Ndipo Eliya anayandikira kwa anthu onse, nati, Mukayika-kayika kufikira liti? ngati Yehova ndiye Mulungu, mtsateni iye; ngati Baala, mumtsate iyeyo. Ndipo anthu nnena kumyankha mau amodzi.

22. Ndipo Eliya ananena ndi anthuwo, Ine ndatsala ndekha mneneri wa Yehova, koma aneneri a Baala ndiwo anthu mazana anai mphambu makumi asanu.

23. Atipatse tsono ng'ombe ziwiri; ndipo adzisankhire iwo eni ng'ombe imodzi, naiduledule, naiike pankhuni osasonkhapo moto; ndipo ine ndidzakonza ng'ombe yinayo, ndi kulika pankhuni osasonkhapo moto.

24. Ndipo muitane inu dzina la mulungu wanu, ine ndidzaitana dzina la Yehova; ndipo Mulunguyo ayankhe ndi mote ndiye Mulungu. Ndipo anthu onse anabvomera, nati, Ndiwo mau abwino amene.

25. Pamenepo Eliya ananena ndi aneneri a Paala, Dzisankhireni ng'ombe imodzi yanu, muyambe kuikonza, popeza mucuruka; nimuitane dzina la mulungu wanu, koma musasonkhepo moto.

1 Mafumu 18