26. Nacita zoipa pamaso pa Yehova, nayenda m'njira ya atate wace, ndi m'chimo lomwelo iye akacimwitsa nalo Aisrayeli.
27. Ndipo Basa mwana wa Akiya, wa nyumba ya Isakara, anampangira ciwembu; ndipo Basa anamkanthira ku Gibetoni wa Afilisti, popeza Nadabu ndi Aisrayeli onse adamangira misasa Gibetoni.
28. Inde Basa anamupha caka cacitatu ca Asa mfumu ya Yuda, nalowa ufumu m'malo mwace.