1 Akorinto 13:3-8 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo ndingakhale ndipereka cuma cangaconsekudyetsa osauka, ndipo ndingakhalendipereka thupi langa alitenthe m'moto, koma ndiribe cikondi, sindipindula kanthu ai.

4. Cikondi cikhala cilezere, ciri cokoma mtima; cikondi sicidukidwa; cikondi sicidziwa kudzitamanda, sicidzikuza,

5. sicicita zosayenera, sicitsata za mwini yekha, sicipsa mtima, sicilingirira zoipa;

6. sicikondwera ndi cinyengo, koma cikondwera ndi coonadi;

7. cikwirira zinthu zonse, cfkhulupirira zinthu zonse, ciyembekeza zinthu zonse, cipirira zinthu zonse.

8. Cikondi sicitha nthawizonse, koma kapena zonenera zidzakhala cabe, kapena malilime adzaleka, kapena nzeru idzakhala cabe.

1 Akorinto 13