1 Akorinto 11:28-32 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

28. Koma munthu adziyese yekha, ndi kotero adye mkate, ndi kumwera cikho.

29. Pakuti iye wakudya ndi wakumwa, adya namwa ciweruziro kwa iye yekha, ngati sazindikira thupilo.

30. Cifukwa cace ambiri mwa inu afoka, nadwala, ndipo ambiri agona.

31. Koma ngati tikadadzizindikira tokha sitikadaweruzidwa.

32. Koma poweruzidwa, tilangidwa ndi Ambuye, kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi dziko lapansi.

1 Akorinto 11