28. Koma munthu adziyese yekha, ndi kotero adye mkate, ndi kumwera cikho.
29. Pakuti iye wakudya ndi wakumwa, adya namwa ciweruziro kwa iye yekha, ngati sazindikira thupilo.
30. Cifukwa cace ambiri mwa inu afoka, nadwala, ndipo ambiri agona.
31. Koma ngati tikadadzizindikira tokha sitikadaweruzidwa.
32. Koma poweruzidwa, tilangidwa ndi Ambuye, kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi dziko lapansi.