1 Akorinto 10:20-27 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Koma nditi kuti zimene amitundu apereka nsembe azipereka kwa ziwanda; ndipo sindifuna kuti inu muyanjane ndi ziwanda.

21. Simungathe kumwera cikho ca Ambuye, ndi cikho ca ziwanda; simungathe kulandirako ku gome la Ambuye, ndi ku gome la ziwanda.

22. Kapena kodi ticititsa nsanje Ambuye? Kodi mphamvu zathu ziposa iye?

23. Zinthu zonse ziloleka; koma sizipindula zonse. Zinthu zonse ziloleka; koma sizimanga zonse.

24. Munthu asafune zace za iye yekha, kama za mnzace.

25. Conse cogulitsidwa pa msika wa nyama, mudye, osafunsa kanthu cifukwa ca cikumbu mtima;

26. pakuti dziko lapansi liri la Ambuye, ndi kudzala kwace.

27. Ngati wina wa osakhulupira akuitanani, ndipo mufuna kupita; mudye comwe ciikidwa kwa inu, osafunsa kanthu, cifukwa ca cikumbu mtima.

1 Akorinto 10