16. Koma ndinabatizanso a pa banja la Stefana; za ena, sindidziwa ngati ndinabatiza wina yense.
17. Pakuti Kristu sanandituma ine kubatiza, koma kulalikira Uthenga Wabwino, si mu nzeru ya mau, kuti mtanda wa Kristu ungayesedwe wopanda pace.
18. Pakuti mau a mtanda ali ndithu cinthu copusa kwa iwo akutayika, koma kwa ife amene tirikupulumutsidwa ali mphamvu ya Mulungu.
19. Pakuti kulembedwa,Ndidzaononga nzeru za anzeru,Ndi kucenjerakwa ocenjera odidzakutha.